Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 31:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yakobo afuna kwao nathawa nazo zace, Ndipo anamva mau a ana ace a Labani kuti, Yakobo watenga zonse za atate wathu; m'zinthu zinali za atate wathu wapeza iye cuma ici conse.

2. Ndipo Yakobo anaona nkhope ya Labani, taonani, siinamuonekera iye monga kale.

3. Ndipo Yehova anati kwa Yakobo, Bwera ku dziko la atate wako, ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakhala ndi iwe.

4. Ndipo Yakobo anatumiza naitana Rakele ndi Leya adze kubusa ku zoweta zace,

5. ndipo anati kwa iwo, Ndiona ine nkhope ya atate wanu kuti siindionekera ine monga kale; koma Mulungu wa atate wanga anali ndi ine.

6. Ndipo inu mudziwa kuti ndi mphamvu zanga zonse ndatumikira atate wanu.

Werengani mutu wathunthu Genesis 31