Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 30:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo Rakele anati, Ndi malimbano a Mulungu ndalimbana naye mkuru wanga, ndipo ndapambana naye; ndipo anamucha dzina lace Nafitali.

9. Pamene Leya anaona kuti analeka kubala, anatenga Zilipa mdzakazi wace, nampatsa iye kwa Yakobo kuti akhale mkazi wace.

10. Ndipo Zilipa mdzakazi wace wa Leya anambalira Yakobo mwana wamwamuna.

11. Ndipo Leyaanati, Wamwai ine! ndipo anamucha dzina lace Gadi.

12. Ndipo Zilipa mdzakazi wa Leya anambalira Yakobo mwana wamwamuna waciwiri.

13. Ndipo Leya anati, Ndakondwa inel cifukwa kuti ana akazi adzandicha ine wokondwa: ndipo anamucha dzina lace Aseri.

Werengani mutu wathunthu Genesis 30