Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 28:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo anacha dzina la pamenepo Beteli; pakuyamba dzina lace la mudziwo ndi Luzi.

20. Yakobo ndipo analumbiracilumbiro, nati, Mulungu akakhala ndi ine, akandisunga ine m'njira imene ndipitamo, akandipatsa ine mkate wa kudya, ndi zobvalira za kubvala,

21. kuti ndibwerenso ku nyumba ya atate wanga ndi mtendere, pamenepo Yehova adzakhala Mulungu wanga,

22. ndi mwala umenewu ndinauimiritsa, udzakhala nyumba ya Mulungu; ndipo la zonse mudzandipatsa ine, ndidzakupatsani Inu limodzi la magawo khumi.

Werengani mutu wathunthu Genesis 28