Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 25:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. ndi Hadada, ndi Tema, ndi Yeturi, ndi Nafisi, ndi Kedema;

16. ana a Ismayeli ndi awa: maina ao m'midzi yao, m'misasa yao ndi awa: akaronga khumi ndi awiri m'mitundu yao.

17. Zaka za moyo wa Ismayeli ndi izi: zaka zana limodzi kudza makumi atatu ndi zisanu ndi ziwiri: ndipo iye anamwalira, natengedwa akhale ndi a mtundu wace.

18. Ndipo anakhala iwo kuyambira ku Havila kufikira ku Suri, ndiko kum'mawa kwace kwa Aigupto, pakunka ku Asuri: ndipo iye anakhala pamaso pa abale ace onse.

19. Mibadwo ya Isake mwana wace wa Abrahamu ndi iyi: Abrahamu anabala Isake:

20. ndipo Isake anali wa zaka makumi anai pamene anakwata Rebeka, mwana wamkazi wa Betuele Msuriya wa ku Padanaramu, mlongo wace wa Labani Msuriya.

Werengani mutu wathunthu Genesis 25