Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 24:21-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Munthuyo ndipo anamyang'anira iye, nakhala cete, kuti adziwe ngati Yehova anamuyendetsa bwino kapena iai.

22. Ndipo panali zitatha kumwa ngamila, munthuyo anatenga mphete yagolidi ya kulemera kwace sekele latheka, ndi zingwinjiri ziwiri za m'manja ace, kulemera kwace masekele khumi a golidi.

23. Ndipo anati, Ndiwe mwana wa yani? Undiuzetu. Kodi ku nyumba ya atate wako kuli malo akuti tigoneko ife?

24. Ndipo mkaziyo anati kwa iye, Ine ndine mwana wa Betuele mwana wamwamuna wa Milika, amene anambalira Nahori.

25. Natinso kwa iye, Tiri nao maudzu ndi zakudya zambiri oeli malo ogona.

26. Munthuyo oelipo anawerama mutu namyamika Yehova.

27. Ndipo anati, Ayamikike Yehova Mulungu wa mbuyanga Abrahamuamene sanasiya mbuyanga wopanda cifundo cace ndi zoona zace: koma ine Yehova Wanditsogolera m'njira ya ku nyumba ya abale ace a mbuyanga.

28. Namwaliyo ndipo anathamanga nawauza zimenezo ku nyumba ya amace.

29. Ndipo Rebeka anali ndi mlongo wace dzina lace Labani; ndipo Labani anathamangira munthuyo kunja ku kasupe.

30. Ndipo panali, pamene anaona mphete ndi zingwinjiri pa manja a mlongo wace, pamene anamva mau a Rebeka mlongo wace, akuti, Cotero ananena ndi ine munthuyo; Labani anafika pa munthuyo; taonani, anaimirira pa ngamila pakasupe.

31. Ndipo anati, Talowa iwe, wodalitsidwa ndi Yehova; uimiriranji kunjako? cifukwa kuti ndakonzeratu nyumba, ndi malo a ngamila.

32. Munthuyo ndipo analowa m'nyumba, namasula ngamila, napatsa ngamila maudzu ndi cakudya, ndi madzi akusamba mapazi ace ndi mapazi a iwo amene anali naye.

33. Ndipo anaika cakudya pamaso pace: koma anati, Sindidzadya ndisananene cimene ndadzera. Ndipo anati, Nenatu.

34. Ndipo anati, Ine ndine mnyamata wa Abrahamu.

35. Yehova wamdalitsa mbuyanga kwambiri; ndipo anakula kwakukuru; ndipo anampatsa iye nkhosa ndi ng'ombe, ndi siliva ndi golidi, ndi akapolo ndi adzakazi, oeli ngamila ndi aburu.

36. Ndipo Sara mkazi wace wa mbuyanga anambalira mbuyanga mwana wamwamuna, mkaziyo anali wokalamba; ndipo anampatsa mwanayo zonse ali nazo.

37. Ndipo mbuyanga anandilumbiritsa ine kuti, Usamteogere mwana wanga mkazi wa ana akazi a Kanani, m'dziko mwao m'mene ndikhala ine;

38. koma udzanke ku nyumba ya atate wanga, kwa abale anga, ndi kumtengera mwana wanga mkazi.

39. Ndipo ndinati kwa mbuyanga, Kapena mkazi sadzanelitsata ine.

40. Ndipo anati kwa ine, Yehova, amene ndiyenda ine pamaso pace, adzatumiza mthenga wace pamodzi ndi iwe, nadzakuyendetsa bwino m'njira yako; ndipo ukamteogere mwana wanga mkazi wa mwa abale anga ndi ku nyumba ya atate wanga;

41. ukatero udzakhala wosacimwa pa malumbiro ako, pofika iwe kwa abate anga; ndipo ngati sadzakupatsa iwe, udzakhala wosacimwa pa malumbiro ako.

Werengani mutu wathunthu Genesis 24