Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 21:26-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo anati Abimeleke, Sindinadziwe amene anacita ico; ndipo iwe sunandiuze ine, ndiponso sindinamve koma lero lino.

27. Ndipo Abrahamu anatenga nkhosa ndi ng'ombe, nampatsa Abimeleke, ndipo anapangana pangano onse awiriwo.

28. Ndipo Abrahamu anapatula ana a nkhosa akazi asanu ndi awiri pa okha.

29. Ndipo Abimeleke anati kwa Abrahamu, Nanga ana a nkhosa akazi asanu ndi awiri amene wapatula pa okha?

30. Ndipo anati, Ana a nkhosa akazi asanu ndi awiriwa uwalandire pa dzanja langa, kuti akhale mboni zanga, kuti ndakumba ine citsime cimeneci.

31. Cifukwa cace anacha malowo Beereseba: cifukwa pamenepo analumbira onse awiri.

32. Ndipo anapangana pangano pa Beereseba: ndipo anauka Abimeleke ndi Fikolo kazembe wa-nkhondo yace, nabwera kunka ku dziko la Afilisti.

33. Ndipo Abrahamu ananka mtengo wabwemba pa Beereseba, naitanira pamenepo dzina la Yehova, Mulungu wa nthawi zonse.

Werengani mutu wathunthu Genesis 21