Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 21:1-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova anayang'anira Sara monga momwe anati, ndipo Yehova anamcitira iye monga ananena.

2. Ndipo Sara anatenga pakati, nambalira Abrahamu m'ukalamba wace mwana wamwamuna, nthawi yomweyo Mulungu anamuuza iye.

3. Ndipo Abrahamu anamucha dzina lace la mwana wace wamwamuna amene anabala iye, amene anambalira iye Sara, Isake.

4. Ndipo Abrahamu anamdula mwana wace wamwamuna Isake pamene anali wa masiku ace asanu ndi atatu, monga Mulungu anamlamulira iye.

5. Ndipo Abrahamu anali wa zaka zana limodzi pamene anambadwira iye Isake mwana wace.

6. Ndipo Sara anati, Mulungu anandisekeretsa ine; onse akumva adzasekera pamodzi ndi ine.

7. Ndipo anati, Akadatero ndani kwa Abrahamu kuti Sara adzayamwitsa ana? pakuti ndambalira iye mwana wamwamuna m'ukalamba wace.

8. Ndipo anakula mwanayo naletsedwa kuyamwa: ndipo Abrahamu anakonza madyerero akuru tsiku lomwe analetsedwa Isake kuyamwa.

9. Ndipo Sara anaona mwana wace wamwamuna wa Hagara M-aigupto, amene anambalira Abrahamu, alinkuseka.

10. Cifukwa cace anati kwa Abrahamu, Cotsa mdzakazi uyo, ndi mwana wace wamwamuna; cifukwa mwana wa mdzakazi uyo sadzalowa m'nyumba pamodzi naye mwana wanga Isake.

11. Ndipo mauwo anaipira Abrahamu cifukwa ca mwana wace.

12. Ndipo Mulungu anati kwa Abrahamu, Usaipidwe nao, cifukwa ca mnyamatayo, ndi cifukwa ca mdzakazi wako; momwe monse akunenera iwe Sara umvere iwe mau ace; cifukwa kuti mwa Isake zidzaitanidwa mbeu zako.

13. Ndipo mwana wamwamuna wa mdzakazi uyo ndidzayesa mtundu, cifukwa iye ndiye mbeu yako.

14. Ndipo Abrahamu analawira m'mamawa, natenga mkate ndi mcenje wa madzi, nampatsa Hagara, naika paphewa pace, ndi mwana, namcotsa iye: ndipo iye anamuka, nasocerera m'cipululu ca Beereseba.

15. Ndipo anatha madzi a m'mcenje ndipo anaika mwana pansi pa citsamba.

Werengani mutu wathunthu Genesis 21