Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 18:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova anamuonekera iye pa mtengo yathundu ya ku Mamre, pamene anakhala pa khomo la hema wace pakutentha dzuwa.

2. Ndipo anatukula maso ace, nayang'ana, taonani, anthu atatu anaima pandunji pace; pamene anaona iwo, anawathamangira kucoka ku khomo la hema kukakomana nao, nawerama pansi, nati,

3. Mbuyanga, ngatitu ndikapeza ufulu pamaso panu, musapitiriretu pa kapolo wanu;

4. nditengetu madzi pang'ono, ndikusambitseni mapazi anu, mupumule pansi pa mtengo;

5. ndipo ndidzatenga cakudya pang'ono, nimutonthoze mitima yanu; mutatero mudzapitirira, cifukwa mwafika kwa kapolo wanu. Ndipo anati, Cita comweco monga momwe wanena.

Werengani mutu wathunthu Genesis 18