Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 17:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi anai kudza zisanu ndi zinai, Yehova anamuonekera Abramu nati kwa iye, Ine ndine Mulungu Wamphamvuyonse; yenda iwe pamaso panga, nukhale wangwiro.

2. Ndipo ndidzapangana pangano langa ndi Ine ndi iwe, ndipo ndidzacurukitsa iwe kwambiri.

3. Ndipo Abramu anagwa nkhope pansi, ndipo Yehova ananena naye kuti,

4. Koma Ine, taona, pangano langa liri ndi iwe, ndipo udzakhala iwe atate wa khamu la mitundu.

5. Sudzachedwanso dzina lako Abramu, koma dzina lako lidzakhala Abrahamu; cifukwa kuti ndakuyesa iwe atate wa khamu la mitundu.

Werengani mutu wathunthu Genesis 17