1. Ndipo Sarai mkazi wace wa Abramu sanambalire iye mwana; ndipo anali ndi mdzakazi, wa ku Aigupto, dzina lace Hagara.
2. Ndipo Sarai anati kwa Abramu, Taonanitu, Yehova anandiletsa ine kuti ndisabale: lowanitu kwa mdzakazi wanga; kapena ndikalandire ndi iye ana. Ndipo Abramu anamvera mau a Sarai.
3. Ndipo Sarai mkazi wace wa Abramu anatenga Hagara mdzakazi wace wa ku Aigupto, Abramu atakhala m'dziko la Kanani zaka khumi, nampereka iye kwa Abramu mwamuna wace, kuti akhale mkazi wace.