Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 15:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo anamturutsa iye kunja, nati, Tayang'anatu kumwamba, uwerenge nyenyezi, ngati ukhoza kuziwerenga zimenezo: ndipo anati kwa iye, Zoterezo zidzakhala mbeuzako.

6. Ndipo anakhulupirira Yehova, ndipo kunayesedwa kwa iye cilungamo.

7. Ndipo anatikwaiye, Ine ndine Yehova amene ndinaturutsa iwe m'Uri wa kwa Akaldayo, kuti ndikupatse iwe dziko limeneli likhale lako lako.

8. Ndipo anati, Ambuye Mulungu, nanga ndidzadziwa bwanji kuti lidzakhala colowa canga?

9. Ndipo anati kwa iye, Kanditengere Ine ng'ombe yaikazi ya zaka zitatu, ndi mbuzi yaikazi ya zaka zitatu, ndi tonde wa zaka zitatu, ndi njiwa, ndi bunda.

10. Ndipo anatenga iye zonse zimenezo, nazidula pakati, naika bandu popenyana ndi linzace: koma mbalame sanazidula.

11. Pamene miimba inatsikira panyama, Abramu anaingitsa iyo.

Werengani mutu wathunthu Genesis 15