Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 15:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. ndiponso mtunduwo adzautumikira, Ine ndidzauweruza: ndiponso pambuyo pace adzaturuka ndi cuma cambiri.

15. Ndipo iwe udzanka kwa makolo ako m'mtendere; nudzaikidwa ndi ukalambawabwino.

16. Koma iwo adzabweranso kuno mbadwo wacinai: pakuti mphulupulu za Aamori sizinakwaniridwe.

17. Ndipo panali pamene litalowa dzuwa ndi kudza mdima, taonani, ng'anjo yofuka utsi ndi muuni wamoto wapita pakati pa mabanduwo.

18. Tsiku lomwelo Yehova anapangana cipangano ndi Abramu, nati, Ndidzapatsa mbeu zako dziko ili, kuyambira pa nyanja ya Aigupto kufikira pa nyanja yaikuru, nyanja ya Firate:

19. Akeni ndi Akenizi, Akadimoni, ndi Ahiti, ndi Aperezi, ndi Arefai, ndi Aamori, ndi Akanani, ndi Agirigasi, ndi Ajebusi.

Werengani mutu wathunthu Genesis 15