Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 13:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo anthu a ku Sodomu anali oipa ndi ocimwa kwambiri pamaso pa Yehova.

14. Ndipo Yehova anati kwa Abramu, atalekana naye Loti, Tukulatu maso ako, nuyang'anire kuyambira kumene uliko, kumpoto, ndi kumwela, ndi kum'mawa, ndi kumadzulo:

15. cifukwa kuti dziko lonse limene ulinkuona, ndidzakupatsa iwe ndi mbeu yako nthawi yonse.

16. Ndipo ndidzayesa mbeu yako monga pfumbi lapansi: cotere kuti ngati munthu angathe kuwerenga pfumbi lapansi, comweconso mbeu yako idzawerengedwa.

17. Tauka, nuyendeyendc m'dzikoli m'litari mwace ndi m'mimba mwace; cifukwa kuti ndidzakupatsa iwe limenelo.

18. Ndipo Abramu anasuntha hema wace nafika nakhala pa mitengo yathundu ya pa Mamre, imene iri m'Hebroni, nammangira Yehova kumeneko guwa la nsembe.

Werengani mutu wathunthu Genesis 13