Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 47:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo mudzakhala nalo colowa canu wina ndi mnzace yemwe, ndilo limene ndinakwezapo dzanja langa kulipereka kwa makolo anu, ndi dziko ili lidzakugwerani colowa canu.

15. Ndipo malire a dzikoli ndi awa: mbali ya kumpoto, kuyambira ku nyanja yaikuru, kutsata njira ya ku Heteloni, kufikira polowera ku Zedadi;

16. Hamati, Berota, Sibraimu, ndiwo pakati pa malire a Damasiko, ndi malire a Hamati; Hazere Hatikoni ndiwo ku malire a Haurani.

17. Ndi malire ocokera kunyanja ndiwo Hazaremoni, ku malire a Damasiko, ndi kumpoto kulinga kumpoto kuli malire a Hamati, Ndiyo mbali ya kumpoto.

18. Ndi mbali ya kum'mawa pakati pa Haurani, ndi Damasiko, ndi Gileadi, ndi dziko la Israyeli, ndiwo Yordano; muyese kuyambira malire a kumpoto kufikira nyanja ya kum'mawa. Ndiyo mbali ya kum'mawa.

19. Ndi mbali ya kumwela kuloza kumwela ndiyo kuyambira ku Tamara kufikira ku madzi a Meriboti Kadesi, ku mtsinje wa Aigupto, ndi ku nyanja yaikuru. Ndiyo mbali ya kumwela kuloza kumwela.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 47