Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 46:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atero Ambuye Yehova, Pa cipata ca bwalo lam'kati coloza kum'mawa patsekedwe masiku asanu ndi limodzi ogwira nchito; koma tsiku la Sabata patsegulidwe, ndi tsiku lokhala mwezi patsegulidwe.

2. Ndipo kalonga azilowera njira ya ku khonde la cipataco, kunja kwace, naime ku nsanamira ya cipata; ndipo ansembe akonze nsembe yace yopsereza, ndi nsembe zace zoyamika, nalambire iye ku ciundo ca cipata; atatero aturuke; koma pacipata pasatsekedwe mpaka madzulo.

3. Ndipo anthu a m'dziko alambire pa citseko ca cipata ici pamaso pa Yehova pamasabata, ndi pokhala mwezi.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 46