Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 43:22-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo tsiku laciwiri upereke tonde wopanda cirema, akhale nsembe yaucimo; ndipo ayeretse guwa la nsembe monga umo analiyeretsera ndi ng'ombeyo.

23. Utatha kuliyeretsa upereke mwana wa ng'ombe wopanda cirema, ndi nkhosa yamphongo ya zoweta yopanda cirema.

24. Ndipo ubwere nazo kwa Yehova, ndi ansembe athirepo mcere, ndi kuzipereka nsembe yopsereza ya Yehova.

25. Masiku asanu ndi awiri uzikonzera mbuzi tsiku ndi tsiku, ikhale nsembe yaucimo; akonzerenso mwana wa ng'ombe, ndi nkhosa yamphongo ya zoweta zopanda cirema.

26. Masiku asanu ndi awiri acite cotetezera guwali ndi kuliyeretsa, momwemo alipatule.

27. Ndipo atatsiriza masiku, kudzacitika tsiku lacisanu ndi citatu ndi m'tsogolo, ansembe azicita nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zanu zoyamika pa guwalo; ndipo ndidzakulandirani, ati Ambuye Yehova.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 43