Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 41:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Mphuthu za Kacisi zinali zamphwamphwa, ndi maonekedwe a pakhomo pa malo opatulika ananga maonekedwe a kacisi.

22. Guwa la nsembe linali lamtengo, msinkhu wace mikono itatu, ndi m'litali mwace mikono iwiri, ndi ngondya zace, ndi tsinde lace, ndi: thupi, nza mtengo; ndipo ananena ndi ine, Ili ndiko gome liri pamaso pa Yehova.

23. Ndipo Kacisi ndi malo opatulikitsa anali nazo zitseko ziwiri.

24. Ndipo pamakomopo panali zitseko zopatukana zotembenuzika, cina copatukana pa khomo lina cina pa linzace.

25. Ndipo panalembedwa pamenepo pa Izitseko za Kacisi akerubi ndi akanjedza, akunga aja adalembedwa pamakhoma; ndipo panali matabwa ocindikira pakhomo pakhonde panja,

26. Ndipo panali mazenera a made okhazikika, ndi akanjedza cakuno ndi cauko, kumbali zace za khonde; momwemonso pa zipinda za m'mphepete mwa nyumba, ndi pa matabwa ocindikira.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 41