Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 41:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndi pakati pa zipinda panali kupingasa kwa mikono makumi awiri, pozungulira pace ponse pa nyumba.

11. Ndi makomo a zipinda za m'mphepete analoza kumpatawo, khomo lina kumpoto, ndi lina kumwela; ndi malo a pa mpatawo anayesa mikono isanu kupingasa kwace pozungulira pace.

12. Ndipo nyumba inali kutsogolo kwa mpata wa mbali ya kumadzulo inali ya mikono makumi asanu ndi awiri kupingasa kwace; ndi khoma la nyumbayo pozungulira pace linali la mikono isanu kucindikira kwace; ndi m'litali mwace mikono makumi asanu ndi anai.

13. Momwemo anayesa kacisi m'litali mwace mikono zana limodzi; ndi mpatawo, ndi nyumbayo, ndi makoma ace, mikono zana limodzi;

14. kupingasa kwace komwe kwa kukhomo kwa nyumba, ndi ku mpatawo kum'mawa, mikono zana limodzi.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 41