Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 40:42-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Ndipo panali magome anai a nsembe yopsereza a miyala yosema, m'litali mwace mkono ndi nusu, kupingasa kwace mkono ndi nusu, msinkhu wace mkono umodzi; pamenepo adafoika zipangizo zimene anaphera nazo nsembe yopsereza ndi nsembe yophera.

43. Ndi ziciri zangowe, cikhato m'litali mwace, zinamangika m'katimo pozungulirapo; ndi pamagome panali nyama ya nsembe.

44. Ndi kunja kwa cipata ca m'kati kunali tinyumba ta oyimba m'bwalo lam'kati, ku mbali ya cipata ca kumpoto; ndipo tinaloza kumwela, kena ku mbali ya cipata ca kum'mawa kanaloza kumpoto.

45. Ndipo anati kwa ine, Kanyumba aka koloza kumwela nka ansembe odikira kacisi.

46. Ndi kanyumba koloza kumpoto nka ansembe odikira guwa la nsembe, ndiwo ana a Zadoki amene ayandikira kwa Yehova mwa ana a Levi, kumtumikira Iye.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 40