Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 39:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo adzasankha anthu akupita-pitabe m'dziko, ndi pamodzi ndi opitapitawo anthu akuika mafupa otsala pamtunda, kuliyeretsa; pakutha miyezi isanu ndi iwiri adzapwaira.

15. Ndipo opitapitawo adzapitapita m'dziko, ndipo winaakaona pfupa la munthu aikepo cizindikilo, mpaka oikawo aliika m'cigwa ca unyinji wa Gogi.

16. Ndipo dzina la mudzi lidzakhala Hamona. Momwemo adzayeretsa dziko.

17. Ndipo iwe, wobadwa ndi munthu, atero Ambuye Yehova, Nena kwa mbalame za mitundu yonse, ndi kwa nyama zonse za kuthengo, Memezanani, idzani, sonkhanani ku mbali zonse, kudza ku nsembe yanga imene ndikupherani, ndiyo nsembe yaikuru pa mapiri a Israyeli, kuti mudzadye nyama ndi kumwa mwazi.

18. Mudzadya nyama ya amphamvu, ndi kumwa mwazi wa akalonga a padziko, wa nkhosa zamphongo, wa ana a nkhosa, ndi wa mbuzi, ndi wa ng'ombe, zonsezi zonenepa za ku Basana.

19. Ndipo mudzadya zonona mpaka mudzakhuta, ndi kumwa mwazi mpaka mudzaledzera za nsembe yanga ndakupherani.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 39