Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 35:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Nandidzeranso mau a Yehova, akuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, Lozetsa nkhope yako ku phiri la Seiri, nulinenere molitsutsa;

3. nuti nalo, Atero Ambuye Yehova, Taona, ndiipidwa nawe phiri la Seiri, ndipo ndidzakutambasulira dzanja langa, ndi kukusanduliza lacipululu ndi lodabwitsa.

4. Ndidzapasula midzi yako, nudzakhala lacipululu; ndipo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

5. Popeza uli nao udani wosatha, waperekanso ana a Israyeli ku mphamvu ya lupanga m'nthawi ya tsoka lao, mu nthawi ya mphulupulu yotsiriza;

6. cifukwa cace, Pali Ine, ati Ambuye Yehova, ndikukonzeratu uphedwe, ndi mwazi udzakulondola; popeza sunadana nao mwazi, mwazi udzakulondola.

7. Ndipo ndidzaika phiri la Seiri lodabwitsa ndi lacipululu, ndi kuononga pomwepo wopitapo ndi wobwerapo.

8. Ndipo ndidzadzaza mapiri ace ndi ophedwa ace pa zitunda zako, ndi m'zigwa zako, ndi m'mitsinje mwako monse; adzagwa ophedwa ndi lupanga.

9. Ndidzakusandutsa mabwinja osatha; ndi m'midzi mwako simudzakhalanso anthu; motero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova,

10. Popeza wanena, Mitundu iwiri iyi ya anthu ndi maiko awiri awa adzakhala anga, tidzakhala nao ngati colowa cathu, angakhale Yehova anali komweko;

11. cifukwa cace, Pali Ine, ati Ambuye Yehova, ndidzacita monga mwa mkwiyo wako, ndi monga mwa nsanje yako unacita nayo pa kukwiya nao iwe; ndipo ndidzadziwika nao pamene ndikuweruza.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 35