1. Ndipo mau a Yehova anandidzera, akuti,
2. Wobadwa ndi munthu iwe, Nenera motsutsa abusa a Israyeli; nenera, nuti nao abusawo, Atero Ambuye Yehova, Tsoka abusa a Israyeli odzidyetsa okha; kodi abusa sayenera kudyetsa nkhosa?
3. Mukudya mafuta, mubvala ubweya, mukupha zonenepa; koma simudyetsa nkhosa.