Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 33:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. nakaona iye lupanga lirikudzera dziko, nakaomba lipenga ndi kucenjeza anthu;

4. ndipo wina, kumva adamva mau a lipenga, koma osalabadira, likadza lupanga, nilimcotsa, wadziphetsa ndi mtima wace.

5. Anamva mau a lipenga, osawalabadira, wadziphetsa ndi mtima wace; akadalabadira, akadalanditsa moyo wace.

6. Koma mlonda akaona lupanga likudza, osaomba lipenga, osacenjeza anthu, nilidza lupanga, nilicotsa mwa iwo; munthu atengedwadi m'mphulupulu zace, koma mwazi wace ndidzaufunsa pa dzanja la mlonda.

7. Iwe tsono, wobadwa ndi munthu, ndakuika mlonda wa nyumba ya Israyeli, m'mwemo imva mau a pakamwa panga, nundicenjezere iwo.

8. Ndikati Ine kwa woipa, Woipawe, udzafa ndithu, osanena iwe kumcenjeza woipayo aleke njira yace, woipa uyo adzafa m'mphulupulu yace, koma mwazi wace ndidzaufunsa pa dzanja lako.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 33