Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 33:23-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

24. Wobadwa ndi munthu iwe, iwo okhala ku mabwinja a dziko la Israyeli anena, ndi kuti, Abrahamu anali yekha, nakhala nalo dziko colowa cace; koma ife ndife ambiri, dzikoli lipatsidwa kwa ife colowa cathu.

25. Cifukwa cace unene nao, Atero Ambuye Yehova, Mumadyera kumodzi ndi mwazi, mumakwezera maso anu ku mafano anu, ndi kukhetsa mwazi; ndipo kodi mudzakhala nalo dziko colowa canu?

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 33