Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 33:14-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo ndikanena kwa woipa, Udzafa ndithu: koma akabwerera iye kuleka cimo lace, nakacita coyenera ndi colungama;

15. woipayo akabweza cikole, nakabweza ico anacilanda mwacifwamba, nakayenda m'malemba a moyo wosacita cosalungama, adzakhala ndi moyo ndithu, sadzafa.

16. Zoipa zace ziri zonse anazicita sizidzakumbukika zimtsutse, anacita coyenera ndi colungama; adzakhala ndi moyo ndithu.

17. Koma ana a anthu a mtundu wako akuti, Njira ya Ambuye siiyenera; koma iwowa njira yao siiyenera.

18. Akabwerera wolungama kuleka cilungamo cace, nakacita cosalungama, adzafa m'mwemo.

19. Ndipo woipa akabwerera kuleka coipa cace, nakacita coyenera ndi colungama, adzakhala ndi moyo nazo.

20. Koma munati, Njira ya Ambuye siiyenera. Nyumba ya Israyeli inu, ndidzakuweruzani, yense monga mwa njira zace.

21. Ndipo kunali caka cakhumi ndi ciwiri ca undende wathu, mwezi wakhumi, tsiku lacisanu la mweziwo, anandidzera wina wopulumuka ku Yerusalemu, ndi kuti, Wakanthidwa mudzi.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 33