Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 33:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, Nena ndi ana a anthu a mtundu wako, uziti nao, Ndikafikitsira dziko liri lonse lupanga, nakatenga eni dziko munthu wa pakati pao, nakamuika awadikirire,

3. nakaona iye lupanga lirikudzera dziko, nakaomba lipenga ndi kucenjeza anthu;

4. ndipo wina, kumva adamva mau a lipenga, koma osalabadira, likadza lupanga, nilimcotsa, wadziphetsa ndi mtima wace.

5. Anamva mau a lipenga, osawalabadira, wadziphetsa ndi mtima wace; akadalabadira, akadalanditsa moyo wace.

6. Koma mlonda akaona lupanga likudza, osaomba lipenga, osacenjeza anthu, nilidza lupanga, nilicotsa mwa iwo; munthu atengedwadi m'mphulupulu zace, koma mwazi wace ndidzaufunsa pa dzanja la mlonda.

7. Iwe tsono, wobadwa ndi munthu, ndakuika mlonda wa nyumba ya Israyeli, m'mwemo imva mau a pakamwa panga, nundicenjezere iwo.

8. Ndikati Ine kwa woipa, Woipawe, udzafa ndithu, osanena iwe kumcenjeza woipayo aleke njira yace, woipa uyo adzafa m'mphulupulu yace, koma mwazi wace ndidzaufunsa pa dzanja lako.

9. Koma ukacenjeza woipa za njira yace, aileke; koma iye osaileka njira yace, adzafa m'mphulupulu mwace iye, koma iwe walanditsa moyo wako.

10. Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, nena kwa nyumba ya Israyeli, Mumatero inu ndi kuti, Zolakwa zathu ndi zocimwa zathu zitikhalira, ndipo ticita nazo liwondewonde, tidzakhala ndi moyo bwanji?

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 33