Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 3:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ananena nane, Wobadwa ndi munthu iwe, Idya cimene wacipeza; idya mpukutu uwu, numuke ndi kunena ndi nyumba ya Israyeli.

2. Pamenepo ndinatsegula pakamwa panga ndipo anandidyetsa mpukutuwo.

3. Nati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, dyetsa m'mimba mwako, nudzaze matumbo ako ndi mpukutu uwu ndakupatsawu. M'mwemo ndinaudya, ndi m'kamwa mwanga munazuna ngati uci.

4. Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, Muka, nufike kwa nyumba ya Israyeli, nunene nao mau anga.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 3