Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 29:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo kunali caka ca makumi awiri mphambu zisanu ndi ziwiri mwezi woyamba, tsiku loyamba la mwezi, anandidzera mau a Yehova, akuti,

18. Wobadwa ndi munthu iwe, Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo anacititsa ankhondo ace nchito yaikuru yoponyana ndi Turo; mitu yonse inacita dazi, ndi mapewa onse ananyuka; koma analibe kulandira mphotho ya ku Turo, iye kapena ankhondo ace, pa nchito anagwirayo;

19. cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Taona, ndidzapereka dziko la Aigupto kwa Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo; ndipo adzacoka nao aunyinji ace, nadzafunkha ndi kulanda zace, ndizo mphotho ya khamu lace.

20. Ndamninkha dziko la Aigupto combwezera nchito yace, popeza anandigwirira nchito, ati Ambuye Yehova.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 29