Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 28:24-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo nyumba ya Israyeli siidzakhalanso nayo mitungwi yolasa, kapena minga yaululu ya ali yense wakuizinga ndi kuipeputsa; motero adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

25. Atero Ambuye Yehova, Pakusonkhanitsa nyumba ya Israyeli mwa mitundu ya anthu anabalalikamo, ndidzazindikirika Woyera mwa iwowa, pamaso pa amitundu; ndipo adzakhala m'dziko mwao mwao ndinalipereka kwa Yakobo mtumiki wanga.

26. Nadzakhalamo osatekeseka, nadzamanga nyumba, ndi kunka mpesa m'mindamo, nadzakhalamo mosatekeseka, ndikatha kukwaniritsira maweruzo pa onse akuwapeputsa pozungulira pao; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wao.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 28