Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 28:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, uziti kwa kalonga wa Turo, Atero Ambuye Yehova, Popeza mtima wako wadzikweza, nuti, Ine ndine mulungu, ndikhala pa mpando wa Mulungu pakati pa nyanja, ungakhale uli munthu, wosati Mulungu, ungakhale waika mtima wako ngati mtima wa Mulungu,

3. taona, ndiwe wanzeru woposa Danieli, palibe cinsinsi angakubisire;

4. mwa nzeru zako ndi luntha lako wadzionerera cuma, wadzionereranso golidi ndi siliva mwa cuma cako;

5. mwa nzeru zako zazikuru ndi kugulana malonda kwako wacurukitsa cuma cako, ndi mtima wako wadzikuza cifukwa ca cuma cako;

6. cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Popeza waika mtima wako ngati mtima wa Mulungu;

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 28