Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 25:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. kuwapereka kwa ana a kum'mawa pamodzi ndi ana a Amoni; ndipo ndidzawapereka akhale ao ao, kuti ana a Amoni asakumbukikenso mwa amitundu;

11. ndipo ndidzakwaniritsa maweruzo m'Moabu; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

12. Atero Ambuye Yehova, Popeza Edomu anacita mobwezera cilango pa nyumba ya Yuda, naparamula kwakukuru pakuibwezera cilango,

13. cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Ndidzatambasulira Edomu dzanja langa, ndi kulilikhira munthu ndi nyama, ndi kulisandutsa labwinja; kuyambira ku Temani mpaka Dedani adzagwa ndi lupanga.

14. Ndipo ndidzalibwezera Edomu cilango mwa dzanja la anthu anga Israyeli; ndipo adzacita m'Edomu monga mwa mkwiyo wanga, ndi ukali wanga; motero adzadziwa kubwezera cilango kwanga, ati Ambuye Yehova.

15. Atero Ambuye Yehova, Popeza Afilisti anacita mobwezera cilango nabwezera cilango ndi mtima wopeputsa kuononga, ndi udani wosatha,

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 25