Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 24:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pakuti mwazi wace uli m'kati mwace anauika pathanthwe poyera, sanautsanulira panthaka kuukwirira ndi pfumbi.

8. Pofuna kuutsa ukali, ndi kubwezera cilango, ndaika mwazi wace pathanthwe poyera, kuti usakwiririke.

9. Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Tsoka mudzi wokhetsa mwazi, ndidzakulitsa mulu wa nkhuni.

10. Zicuruke nkhuni, kuleza moto, nyama ipse, uwiritse msuzi wace, ubwadamuke, ndi mafupa ace atibuke.

11. Pamenepo uukhazike pa makara ace opanda kanthu m'menemo, kuti utenthe, nuyake mkuwa wace; ndi kuti codetsa cace cisungunuke m'mwemo, kuti dzimbiri lace lithe.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 24