Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 23:45-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

45. Ndipo anthu olungama adzawaweruza monga mwa maweruzo a acigololo, ndi maweruzo a akazi okhetsa mwazi; pakuti ndiwo acigololo, ndi m'manja mwao muli mwazi.

46. Pakuti atero Ambuye Yehova, Ndidzawakweretsera msonkhano wa anthu, ndi kuwapereka awazunze, ndi kulanda cuma cao.

47. Ndi msonkhanowo udzawaponya miyala, ndi kuwatha ndi malupanga ao, adzawapha ana ao amuna ndi akazi, ndi kutentha nyumba zao ndi moto.

48. Momwemo ndidzaleketsa dama m'dzikomo, kuti alangizidwe akazi onse kusacita monga mwa dama lanu.

49. Ndipo adzakubwezerani dama lanu, nimudzasenza macimo a mafano anu; motero mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 23