Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 22:11-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo wina anacita conyansa ndi mkazi wa mnansi wace, winanso wadetsa mpongozi wace mwamanyazi, ndi wina mwa iwe anaipitsa mlongo wace mwana wamkazi wa atate wace.

12. Analandira mphotho mwa iwe kukhetsa mwazi, walandira phindu loonjezerapo, wanyengerera anansi ako ndi kuwazunza, ndipo wandiiwala Ine, ati Ambuye Yehova.

13. Taona, ndaomba manja pa phindu lako lonyenga waliona, ndi pa mwazi wokhala pakati pako.

14. Mtima wako udzaimika kodi, manja ako adzalimbikira masikuwo ndidzacita nawe? Ine Yehova ndanena, ndidzacicita.

15. Ndipo ndidzakumwaza mwa amitundu, ndi kukubalalitsa m'maiko, ndi kukuthera zodetsa zako zikucokere.

16. Ndipo udzaipsidwa mwa iwe wekha pamaso pa amitundu; motero udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

17. Ndipo mau a Yehova anandidzera, akuti,

18. Wobadwa ndi munthu iwe, nyumba ya Israyeli yandikhalira mphala; onsewo ndiwo mkuwa, ndi seta, ndi citsulo, ndi ntobvu, m'kati mwa ng'anjo; ndiwo mphala zasiliva.

19. Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Popeza mwasanduka mphala nonsenu, cifukwa cace taonani, ndidzakusonkhanitsani m'kati mwa Yerusalemu.

20. Monga asonkhanitsamtapo wa siliva, ndi mkuwa, ndi citsulo, ndi ntobvu, ndi seta, m'kati mwa ng'anjo, kuzibvukutira moto, kuzisungunula momwemo, ndidzakusonkhanitsani mu mkwiyo wanga ndi ukali wanga, ndi kukuikani komweko, ndi kukusungunulani.

21. Inde ndidzakusonkhanitsani, ndi kukubvukutirani ndi moto wa kuzaza kwanga, ndipo mudzasungunuka pakati pace.

22. Monga siliva asungunuka m'kati mwa ng'anjo, momwemo inu mudzasungunuka m'kati mwace; motero mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakutsanulirani ukali wanga.

23. Nandidzeranso mau a Yehova, akuti,

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 22