Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 21:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Pfuula ndi kulira, wobadwa ndi munthu iwe, pakuti likhalira pa anthu anga, likhalira pa akalonga onse a Israyeli, laperekedwa kulupanga pamodzi ndi anthu anga; cifukwa cace panda pancafu pako.

13. Pakuti pali kuyesedwa; ndipo nanga ndodo yacifumu yopeputsa ikapanda kukhalanso? ati Ambuye Yehova.

14. Ndipo wobadwa ndi munthu iwe, nenera, nuombe manja, lupanga lipitirize katatu, lupanga la wolasidwa ndilo lupanga la wolasidwa wamkuruyo, limene liwazinga.

15. Ndalozetsa nsonga ya lupanga ku zipata zao zonse, kuti mtima wao usungunuke, ndi kukhumudwa kwao kucuruke; ha! analituula linyezimire, analisongoza liphe,

16. Udzisonkhanitsire pamodzi, muka ku dzanja lamanja; undandalitsa nkhondo kumuka kulamanzere; kuli konse ilozako nkhope yako.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 21