Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 20:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo ndinawapatsanso masabata anga akhale cizindikilo pakati pa Ine ndi iwo, kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova wakuwapatula.

13. Koma nyumba ya Israyeli inapaodukira Ine m'cipululu, sanayenda m'malemba anga, nanyoza maweruzo anga, amene, munthu akawacita adzakhala nao ndi moyo; ndi masabata anga anawaipsa kwambiri; pamenepo ndidati ndiwatsanulire ukali wanga m'cipululu kuwatha.

14. Koma ndinacicita cifukwa ca dzina langa, kuti lisaipsidwe pamaso pa amitundu amene ndinawaturutsa pamaso pao.

15. Ndipo ndinawakwezeranso dzanja langa m'cipululu, kusawalowetsa m'dzikolo ndidawapatsa, moyenda mkaka ndi uci, ndilo lokometsetsa mwa maiko onse;

16. popeza ananyoza maweruzo anga, osayenda m'malemba anga, naipsa masabata anga; pakuti mitima yao inatsata mafano ao.

17. Koma diso langa lidawaleka osawaononga, sindinawatha onse m'cipululu.

18. Ndipo ndinati kwa ana ao m'cipululu, Musamayenda m'malemba a atate anu, musawasunga maweruzo ao, kapena kudzidetsa ndi mafano ao;

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 20