Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 16:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo popita Ine panali iwepo, ndinakuona ulikubvimvinizika m'mwazi wako. Pamenepo ndinanena ndi iwe m'mwazi wako, Khala ndi moyo, inde ndinati kwa iwe m'mwazi mwako, Khala ndi moyo.

7. Ndinakucurukitsa ngati mphundu za kumunda; ndipo unathululuka ndi kukula kufikira wakongola nkhope, maere ako anamera, ndi tsitsi lako linamera; koma unali wamarisece ndi wausiwa.

8. Ndipo popita Ine panali iwepo ndi kukupenya, taona nyengo yako ndiyo nyengo yakukondana; pamenepo ndinakupfunda copfunda canga, ndi kuphimba umarisece wako; inde ndinakulumbirira ndi kupangana nawe, ati Ambuye Yehova, ndipo unakhala wanga.

9. Ndipo ndinakusambitsa ndi madzi, inde ndinakutsuka kukucotsera mwazi wako, ndi kukudzoza mafuta.

10. Ndinakubvekanso ndi nsaru zopikapika, ndi kukubveka nsapato za cikopa ca katumbu; ndinakuzenenga nsaru yabafuta, ndi kukuphimba ndi nsaru yasilika.

11. Ndinakukometseranso ndi zokometsera, ndi kuika zigwinjiri m'manja mwako, ndi unyolo m'khosi mwako.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 16