Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 13:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mau a Yehova anandidzera ine, akuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, Unenere za aneneri a Israyeli onenerawo, nuziti nao onenera za m'mtima mwao mwao, Tamverani mau a Yehova.

3. Atero Ambuye Yehova, Tsoka aneneri opusawo akutsata mzimu wao wao, cinkana sanaona kanthu.

4. Aneneri ako, Israyeli, akhala ngati nkhandwe m'mapululu.

5. Simunakwera kuima mopasuka, kapena kumanganso linga la nyumba ya Israyeli, kuima kunkhondo tsiku la Yehova.

6. Iwo aona zopanda pace, ndi phenda labodza amene anena, Atero Yehova; koma Yehova sanawatuma, nayembekezetsa anthu kuti mauwo adzakhazikika.

7. Simunaona masomphenya opanda pace kodi? simunanena ula wabodza kodi? pakunena inu, Atero Yehova; cinkana sindinanena?

8. Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Popeza mwanena zopanda pace, ndi kuona mabodza, cifukwa cace taonani, ndikhala Ine wotsutsana nanu, ati Ambuye Yehova.

9. Ndi dzanja langa lidzakhala lotsutsana nao aneneri akuona zopanda pace, ndi kupenda za bodza; sadzakhala mu msonkhano wa anthu anga, kapena kulembedwa m'buku lolembedwamo nyumba ya Israyeli, kapena kulowa m'dziko la Israyeli; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova,

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 13