Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 12:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Anandidzeranso mau a Mulungu, akuti,

18. Wobadwa ndi munthu iwe, udye mkate wako ndi kunthunthumira, ndi kumwa madzi ako ndi kunjenjemera, ndi kutenga nkhawa;

19. nunene kwa anthu a m'dziko, Atero Yehova Mulungu za iwo okhala m'Yerusalemu, ndi za dziko la Israyeli, Adzadya mkate wao ndi nkhawa, ndi kumwa madzi ao ndi kusumwa; pakuti dziko lao lidzakhala lacipululu, kuleka kudzala kwace cifukwa ca ciwawa ca onse okhalamo.

20. Ndi midzi yokhalamo anthu idzapasuka, ndi dziko lidzakhala labwinja; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

21. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 12