Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 12:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mau a Yehova anandidzeranso, ndi kuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, ukhala pakati pa nyumba yampanduko, yokhala nao maso akuonera, koma osaona; ndi makutu akumvera, koma osamva; pakuti iwo ndiwo nyumba yampanduko.

3. Potero wobadwa ndi munthu iwe, udzikonzeretu akatundu a pa ulendo wa kundende, nucoke usana pamaso pao, ucoke pakhala iwepo kumka malo ena pamaso pao; kapena adzacizindikira, angakhalendiwo nyumbayopanduka.

4. Uziturutsa akatundu ako usana pamaso pao, ngati a pa ulendo wa kundende; ndipo madzulo uzituruka wekha pamaso pao, monga amaturuka olowa kundende.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 12