8. Mwaopa lupanga, tsono ndidzakufikitsirani lupanga, ati Yehova Mulungu.
9. Ndipo ndidzakuturutsani m'kati mwace, ndi kukuperekani m'manja a alendo, ndi kucita maweruzo pakati panu.
10. Mudzagwa ndi lupanga, ndidzakuweruzirani ku malire a Israyeli; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
11. Mudzi uno sudzakhala mphika wanu, ndi inu simudzakhala nyama m'kati mwace, ndidzakuweruzirani ku malire a Israyeli;
12. ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pakuti simunayenda m'malemba anga, kapena kucita maweruzo anga, koma mwacita monga mwa maweruzo a amitundu okhala pozungulira panu.