Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 11:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Mwaopa lupanga, tsono ndidzakufikitsirani lupanga, ati Yehova Mulungu.

9. Ndipo ndidzakuturutsani m'kati mwace, ndi kukuperekani m'manja a alendo, ndi kucita maweruzo pakati panu.

10. Mudzagwa ndi lupanga, ndidzakuweruzirani ku malire a Israyeli; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

11. Mudzi uno sudzakhala mphika wanu, ndi inu simudzakhala nyama m'kati mwace, ndidzakuweruzirani ku malire a Israyeli;

12. ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pakuti simunayenda m'malemba anga, kapena kucita maweruzo anga, koma mwacita monga mwa maweruzo a amitundu okhala pozungulira panu.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 11