Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 4:18-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Kalatayo mwatitumizira anandiwerengera momveka.

19. Ndipo ndinalamulira anthu, nafunafuna, napeza kuti mudzi uwu unaukira mafumu kuyambira kale lomwe ndi kuti akacitamo mpanduko ndi kudziyendera.

20. Panalinso mafumu amphamvu m'Yerusalemu amene anacita ufumu tsidya lija lonse la mtsinje, ndipo anthu anawapatsa msonkho, thangata, ndi msonkho wa m'njira.

21. Mulamulire tsono kuti anthu awa aleke, ndi kuti asamange mudzi uwu, mpaka ndidzalamulira ndine.

22. Cenjerani mungadodomepo, cidzakuliranji cisauko ca kusowetsa mafumu?

23. Pamenepo atawerenga malemba a kalata wa mfumu kwa Rehumu, ndi Simsai mlembi, ndi anzao, anafulumira kupita ku Yerusalemu kwa Ayuda, nawaletsa ndi dzanja lamphamvu.

24. Momwemo inalekeka nchito ya nyumba ya Mulungu yokhala ku Yerusalemu; nilekeka mpaka caka caciwiri ca ufumu wa Dariyo mfumu ya Perisiya.

Werengani mutu wathunthu Ezara 4