Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 4:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Adziwe mfumu kuti, Ayuda adakwerawo ocokera kwanu atifikira ife ku Yerusalemu, alikumanga mudzi uja wopanduka ndi woipa, alikutsiriza malinga ace, nalumikiza maziko ace.

13. Adziwe tsono mfumu, kuti akamanga mudzi uwu ndi kutsiriza malinga ace, sadzapereka msonkho, kapena thangata, kapena msonkho wa m'njira; ndipo potsiriza pace kudzasowetsa mafumu.

14. Popeza tsono timadya mcere wa m'nyumba ya mfumu, sitiyenera kungopenyerera mpepulo wa pa mfumu; cifukwa cace tatumiza ndi kudziwitsa mfumu,

15. kuti afunefune m'buku la cikumbutso la makolo anu; momwemo mudzapeza m'buku la cikumbutso, ndi kudziwa kuti mudzi uwu ndi mudzi wopanduka, ndi wosowetsa mafumu, ndi maiko; ndi kuti amadziyendera m'menemo kuyambira kale lomwe; ndico cifukwa cakuti anapasula mudzi uwu.

Werengani mutu wathunthu Ezara 4