Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 4:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. ndi amitundu otsala amene, Osinapera wamkuru ndi womveka adawatenga mikoli, nawakhalitsa m'mudzi wa Samariya, ndi m'dziko lotsala tsidya lino la mtsinje wa Firate, pa nthawi yakuti.

11. Zolembedwa m'kalatayo anamtumiza kwa Aritasasta mfumu ndizo: Akapolo anu, anthu a tsidya lino la mtsinjewo, ndi pa nthawi yakuti.

12. Adziwe mfumu kuti, Ayuda adakwerawo ocokera kwanu atifikira ife ku Yerusalemu, alikumanga mudzi uja wopanduka ndi woipa, alikutsiriza malinga ace, nalumikiza maziko ace.

13. Adziwe tsono mfumu, kuti akamanga mudzi uwu ndi kutsiriza malinga ace, sadzapereka msonkho, kapena thangata, kapena msonkho wa m'njira; ndipo potsiriza pace kudzasowetsa mafumu.

14. Popeza tsono timadya mcere wa m'nyumba ya mfumu, sitiyenera kungopenyerera mpepulo wa pa mfumu; cifukwa cace tatumiza ndi kudziwitsa mfumu,

Werengani mutu wathunthu Ezara 4