Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 2:68-70 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

68. Ndipo akulu ena a nyumba za makolo, pofika ku nyumba ya Yehova iri ku Yerusalemu, anapereka caufulu kwa nyumba ya Mulungu cakulimika pakuzika pace.

69. Monga momwe anakhoza anapereka ku cuma ca nchitoyi madariki agolidi: zikwi zisanu ndi cimodzi, miyeso ya siliva zikwi zisanu, ndi maraya a ansembe zana limodzi.

70. Ndipo ansembe, ndi Alevi, ndi anthu ena, ndi oyimbira, ndi odikira, ndi Anetini, anakhala m'midzi mwao, ndi Aisrayeli onse m'midzi mwao.

Werengani mutu wathunthu Ezara 2