Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 10:16-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Pamenepo anthu otengedwa ndende anacita cotero. Ndi Ezara wansembe, ndi anthu akuru a nyumba za makolo, monga mwa nyumba za makolo ao, iwo onse ochulidwa maina ao anasankhidwa, nakhala pansi tsiku loyamba la mwezi wakhumi kufunsa za mlanduwu.

17. Natsiriza nao amuna onse adadzitengera akazi acilendo tsiku loyamba la mwezi woyamba.

18. Ndipo anapeza mwa ana a ansembe odzitengera akazi acilendo, ndiwo a ana a Yesuwa mwana wa Yozadaki, ndi abale ace Maseya, ndi Eliezere, ndi Yaribu, ndi Gedaliya.

Werengani mutu wathunthu Ezara 10