Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 9:32-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Koma tirigu ndi rai sizinayoyoka popeza amabzala m'mbuyo.

33. Ndipo Mose anaturuka kwa Farao m'mudzi nasasatulira manja ace kwa Yehova; ndipo mabingu ndi matalala analeka, ndi mvula siinabvumbanso padziko.

34. Pamene Farao anaona kuti mvula ndi matalala ndi mabingu zidaleka anaonjezanso kucimwa, naumitsa mtima wace, iye ndi anyamata ace.

35. Potero mtima wa Farao unalimba, ndipo sanalola ana a Israyeli amuke; monga Yehova adalankhula mwa Mose.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 9