Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 9:22-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tambasula dzanja lako kuthambo, kuti pakhale matalala pa dziko lonse la Aigupto, pa anthu ndi pa zoweta, ndi pa zitsamba zonse za kuthengo, m'dziko la Aigupto.

23. Pamenepo Mose anasamulira ndodo yace kuthambo, ndipo Yehova anatumiza bingu ndi matalala, ndi moto unatsikira pansi; ndipo Yehova anabvumbitsa matalala pa dziko la Aigupto.

24. Potero panali matalala, ndi mota wakutsikatsika pakati pa matalala, coopsa ndithu; panalibe cotere m'dziko lonse la Aigupto ciyambire mtundu wao.

25. Ndipo matalala anapanda m'dziko lonse la Aigupto zonse za pabwalo, kuyambira anthu kufikira zoweta; ndipo matalala anapanda zitsamba zonse za kuthengo, nathyola mitengo yonse ya kuthengo.

26. M'dziko la Goseni mokha, mokhala ana a Israyeli, munalibe matalala.

27. Ndipo Farao anatumiza, naitana Mose ndi Aroni, nanena nao, Ndacimwa tsopano; Yehova ndiye wolungama, ine ndi anthu anga ndife oipa,

28. Pembani kwa Yehova; cifukwa akwanira ndithu mabingu a Mulungu ndi matalala; ndipo ndidzakulolani mumuke, osakhalanso.

29. Ndipo Mose ananena naye, Poturuka m'mudzi ine, ndidzasasatulira manja anga kwa Yehova; mabingu adzaleka, ndi matalala sadzakhalaponso; kuti mudziwe kuti dziko lapansi nla Yehova.

30. Koma inu ndi anyamata anu ndidziwa kuti simudzayamba kuopa nkhope ya Yehova Mulungu.

31. Ndipo thonje ndi barele zinayoyoka; pakuti barele lidafura, ndi thonje lidayamba maluwa.

32. Koma tirigu ndi rai sizinayoyoka popeza amabzala m'mbuyo.

33. Ndipo Mose anaturuka kwa Farao m'mudzi nasasatulira manja ace kwa Yehova; ndipo mabingu ndi matalala analeka, ndi mvula siinabvumbanso padziko.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 9