Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 8:27-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Timuke ulendo wa masiku atatu m'cipululu, tikamphere Yehova Mulungu wathu nsembe, monga adzanena nafe.

28. Ndipo Farao anati, Ndidzakulolani mumuke, kuti mukamphere nsembe Yehova. Mulungu wanu m'cipululu; komatu musamuke kutaritu: mundipembere.

29. Ndipo Mose anati, Onani, ndirikuturuka ine kwanu, ndidzapemba Yehova kuti mizaza icoke mawa kwa Farao, ndi kwa anyamata ace, ndi kwa anthu ace; komatu, Farao asanyengenso ndi kukana kulola anthuwa amuke kukamphera nsembe Yehova.

30. Ndipo Mose anaturuka kwa Farao, napemba Yehova.

31. Ndipo Yehova anacita monga mwa mau a Mose; nacotsera Farao ndi anyamata ace ndi anthu ace mizazayo, sunatsala ndi umodzi wonse.

32. Koma Farao anaumitsa mtima wace nthawi yomweyonso, ndipo sanalola anthu amuke.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 8