Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 7:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, ndi kuti,

9. Pamene Farao adzalankhula nanu, ndi kuti, Dzicitireni codabwiza; pamenepo uzinena ndi Aroni, Tenga ndodo yako, Iponye pansi pamaso pa Farao, isanduke cinjoka,

10. Ndipo Mose ndi Aroni analowa kwa Farao, nacita monga momwe Yehova adawalamulira; ndipo Aroni anaponya pansi ndodo yace pamaso pa Farao, ndi pamaso pa anyamata ace, ndipo inasanduka cinjoka,

11. Pamenepo Farao anaitananso anzeru, ndi amatsenga; ndipo alembi a Aigupto, iwonso anacita momwemo ndi matsenga ao.

12. Pakuti yense anaponya pansi ndodo yace, ndipo zinasanduka zinjoka; koma ndodoya Aroni inameza ndodo zao,

13. Koma mtima wa Farao unalimba, ndipo sanamvera iwo; monga adalankhula Yehova.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 7